NGATI BWANDE WA LERO PA MIJ FM WAKUPHONYANI KAMBA KA VUTO LA - TopicsExpress



          

NGATI BWANDE WA LERO PA MIJ FM WAKUPHONYANI KAMBA KA VUTO LA MAGETSI,WA LERO NDI AMENEYU #Achimwene, Zochitikazo kwathu kuno ndiye ndisaname zikukhala ngati tsopano zachepa, moti awo amene anazolowera kuyenda nthawi imene ija ndi mama Jo, naonso akuchita kudabwa kuti koma abale chikuchitika ndi chiyani? Mzimayi wina aliyense amene anachembezako amayembekezera kuti mwana amene ali kumbuyo kwake nthawi zina adziti akakhalakhala adzilirako, iye nkutenga ka mkute nkumponyera amveke “Eeh, takwaya, mwina usiye kulirako” Koma mwana nthawi zonse akamangoti ziii, zimakayikitsa. Mzimayi nthawi zina amadzifunsa kuti koma mwana wangayu ndi zenizeni? Kodi mwana wangayu koma ndithu adzakula nkukhala munthu olongosoka? Masiku akupita tsopano, koma kwathu kuno kuli ziii. Chiyembekezo chimene chinalipo pakatipa kuti mwina mwake zinthu kwathu kuno zikasintha ndiye kuti zambirinso zisintha mukanthawi kochepa. Tinali ndi chiyembekezo kuti mwina nkutheka Mama Jo amalephera zambiri, koma a bulazi akangofika zinthu nthawi yomweyo zisinthiratu. Moyo wathu okhalira phanthi umene takhala tikukhala usinthiratu, ambanda amene pakatipa amadzitama kuti kamba koti omba ipha “Shoot to Kill” inatha mwina zinthu zikasintha naonso aona polekera. Tinali ndi chiyembekezo chonse kuti zinthu zikangosintha, achinyamata athu, ulendo wa a Kafadala amene nthawi zambiri amakhala akukangalika ndi abulazi nthawi ija apezeredwa ntchito mwamsangamsanga monga mwalonjezo. Chiyembekezo chinalipo kuti chitonzo chimene chinali pamaso pathu m’mbuyomu tsopano chichoka, ndipo anthu ayamba kutiona ngati anthu. Koma ayi ndithu achimwene, zikuoneka kuti tinawerengera kwambiri madzi amphutsi. Masiku angapo tsopano apita, koma zikumakhala zinthu zondivuta kuti ndiloze kuti kodi chenicheni chamzeru chimene ena aja amakanika chimene tsopano chachitika mwamsangamsanga ndi chiti? Zikumakhala zondivuta kwambiri m’masiku amene apitawa kutri ndiloze kuti koma ichitu chachitika chifukwa chamzeru za uje. Pakadali pano achimwene chachilendo chimene chikuchitika kwathu kuno ndikuchotsana, ndikulembana ntchito basi. Ndiye ntchito yotamandika imene ikuchitika pakadali pano. Zilibe kanthu kuti kaya amene akulembedwa ntchitowo ndiotani, koma ndithu ndi zimene zikuchitika pakadali pano. Mwinatu mukumanyogodola kuti “OBwande, mwinatu mukunyasidwa chifukwa dzina lanu silili nawo mumndandanda wa awo osankhidwawo” Ayi ndithu achimwene, ifeyo zosankhanazi tilibe nazo ntchito, ndipo m’moyo mwathu monse sitinaloteko. Ife paja atatichotsa ntchito kukampani ija yoomba nsalu nthawi ija tinaona kuti basi, kulibwino kumalima kuno kumudzi kuchikumbeni. Zomakhalanso tili jagalijagali kupembedzera ntchito ayi ndithu, nthawi imeneyo tilibe. Kungoti nthawi zina zake timangokhala odabwitsika kuti anthu ena ndithu samaphunzirapo zinthu zina zikamachitika m’mbuyomu. Nthawi ya Big Man, zochitikachitika zake zinali zomwezo, anthu ochuluka amene anali ndi zowayenereza kugwira ntchito zosiyanasiyana anachitsedwa ntchito kamba koti sanali mbali yawo, ena analembedwa ntchito angakhale analibe zowayenereza, ndiye zotsatira zake kunali kukasakaza ndalama zathu zamisonkho. Big Man atapita, kunabweranso Mama Jo amene naonso anachita chimodzimodzi, onse amene amaoneka kuti amapanga za Big man kunali kusesa, kufuna kuona zina. Anthu anadandaula, ndipo ena anaona ngati mwina oobwera mtsogolomu adzatengerapo phunziro. Lero lino kubwera abulazi, ndiye kusesanso osati masewera. Munthawi yochepa, koma alira kuti ntchito zawo zatha nkukhalanso miyandamiyanda. Kumafika popereka mantha kuti kom abale, kuti kuthere zaka zisanuko, kukhalabe anthu m’malo athu ogwira ntchitowa? Achimwene a Dodolido, kwathu kunotu zafika poti tikumachita kuwerenga kuti auje apita, pano atsala auje. Pano moti mutandifunsa kuti kodi watsala ndi ndani ndi ndani kuti achotsedwe, ndikhoza kukuuzani mayina onse mosavuta. Achotsedwabe basi. Zilibe kanthu kuti kaya ntchito amayidziwa, kaya ndi ophunzira bwanji, koma ngati nthawi ina yake anaombapo m’manja Mama Jo atalankhula zina zake ameneyo ndiye kuti ndi mzawo wa Mama Jo akuyenera kupita basi. Ine okhala mnyasa zimandikhudza kwambiri achimwene. Ndimadzifunsa kuti koma basi, imeneyo ndiye ntchito imene tingagwire? Kuchotsa ndikulemba basi? Pena anthu kumafika pomadzifunsa kuti koma brother Leader wathuyu alipo? Iiiih, koma ndiye wasowatu, akutsogoleradi ndi iye eti? Kkkkk Timaona ngatitu tili pa auto pilot. Iyayi dyamani zina zake bwezi akumachitako, kuti mwina tioneko kuti ayi kwabweradi mzeru zina zatsopano, nanga kungoti ziiii! Naye Bebe paja nayenso anati ziii. Sikono ili mkamwa akulephera kulankhula Bebe. Mwina mwake kutsogoloku adzabwera kudzatiuuzanso za Agenda for Change, koma pano akadadyererabe manyong’olometsi ampando onona. Koma amzakefe akutikumbukira kaya? Anatisiyatu padzuwa, koma paja nthawi ijayo tinkalimbitsana mitima tonse kuti zinthu zikhala bwino ndi Agenda for Change, tsopano chimene chinachitika mu Agenda for Change ndi chiyani? Ndalama ndi ina yake sungayimvetse amwene! Bolani obusa, obambo otambala naonso asati alandire katambala nkukhazikika pansi. Kuchita za olenga mafuta satuwa. Kuti kwathu kuno zinthu ziyende ndithudi tikufunika anthu ena omayima pachulu ndikudzudzula ziinthu zikamalakwika. Mphamvu zambiri ndizoopsa, zimaononga zambiri. Tazionako m’mbuyomu….amzawo a bulazi akangoyamba kumera mapiko, amadzayamba kuderera tsopano kuti palibe angamuope. Mzimayi opanda ndi dzina lomwe, koma chifukwa choti wavala nkhope ya abulazi komanso makaka ampingo wawo amatha kumuderera ndithu wachitetezo kumasankho osankha mfumu ya mzinda, kumuuza wachitetezo kuti wachepa mphwanga wamva? Ife tavutikatu , mdziko muno kwambiri. Naye wachitetezo pokumbukira zikwanje zimene zinkayenda m’mbuyomu amadzangokhalanso chete ! ine monga mzika yokhudzidwa, ndikumapemphera kuti zimenezi zisadzachutikenso mdziko mwathu muno, kuti anthu wamba nkukhala ndi mphamvu zambiri kuposa mapholisa athu, kumapanga zinthu zimene akufuna mdzina lampingo. Mantha anga ndi oti zimene zija zikayambiranso, ndiye kutitu palibenso kusiyana, m’malo mopita chitsogolo tikhala tikubwerera m’mbuyo! Chonde abulazi, musangokhala chete, chitanipo kanthu abulazi, tiyamba kudabwatu ndikumayimba nyimbo ndimanena ija…ukudzifunsa kuti itiyo? Hahahaha! Usanditole mkamwa ine Bwantasa wabwinobwino.
Posted on: Fri, 11 Jul 2014 08:46:51 +0000

Trending Topics



563786240456">. What more can be expected from SP + Congress-I rule in India? .
Seems that the BLM still does not want to follow the laws of the
Craft books for sale. All prices based on ebay/amazon user

Recently Viewed Topics




© 2015